Sitisiya

Sitisiya

Pangani Dawunilodi:

  1. 1. Nditamva cho’nadi koyamba

    Za Yehova ndi za paradaiso,

    N’nayamba kuzikonda kwambiri.

    M’dzikoli zosokoneza n’zambiri.

    (KUKONZEKERA KOLASI)

    Sindingasiye,

    N’zichita zoyenera.

    (KOLASI)

    Ndikulimbitsa chikhulupiriro.

    Sindidzabwerera m’mbuyo.

    Mawu ake anditsogolere.

    Ndikupempha ndipirire.

    Ndikhale wolimba, sindisiya.

  2. 2. Tikhozatu kusankha mwanzeru

    Polimbitsa chikhulupiriro.

    Dzikoli likufuna tisinthe

    Ndikumachita zomwe tikufuna.

    (KUKONZEKERA KOLASI)

    Posachedwatu,

    Dziko likupita.

    (KOLASI)

    Tikulimbitsa chikhulupiriro.

    Sitidzabwerera m’mbuyo.

    Mawu ake atitsogolere.

    Tikupempha tipirire.

    Tikhale olimba, sitisiya.

    (KOLASI)

    Tikulimbitsa chikhulupiriro.

    Sitidzabwerera m’mbuyo.

    Mawu ake atitsogolere.

    Tikupempha tipirire.

    Tikhale olimba, sitisiya.

    Sitisiya.

    Sitisiya.