Mbiri ya Baibulo
Zimene Zinachitika Kuti Baibulo Lisungike Mpaka Pano
Sitikukayikira kuti mfundo zimene zinali mʼmipukutu yoyambirira ya Baibulo zinakopedwa molondola nʼkusungidwa mpaka pano.
Baibulo Linasungidwa Ngakhale Kuti Ena Ankalitsutsa
Atsogoleri andale komanso azipembedzo akhala akuletsa anthu kumasulira, kusindikiza ngakhalenso kukhala ndi Baibulo, koma sizinatheke.
Kodi Tingadziwe Bwanji Kuti Baibulo Limanena Zoona?
Ngati Baibulo linachokeradi kwa Mulungu, ndiye kuti liyenera kukhala losiyana kwambiri ndi mabuku ena onse.
Kodi Baibulo Linasinthidwa Kapena Kusokonezedwa?
Popeza kuti Baibulo ndi buku lakalekale, kodi tingatsimikize bwanji kuti uthenga wake ndi wolondola mpaka pano?
Baibulo Linapulumuka Ngakhale Kuti Ena Ankafuna Kusintha Uthenga Wake
Anthu amaganizo olakwika ankafuna kusintha uthenga wa m’Baibulo. Koma zolinga zawozi zinadziwika ndiponso zinalephereka?